Mutu 15
1Pamenepo alembi ndi Afarisi ochokera ku Yerusalemu anabwera kwa Yesu, nanena, 2Chifukwa chiyani ophunzira anu amaphwanya lamulo limene linaikidwa ndi makolo akale1? Pakuti iwo sasamba m'manja mwao pamene akudya mkate. 3Koma Iye poyankha anati kwa iwo, Chifukwa chiyaninso inu mumaphwanya lamulo la °Mulungu potsata chiphunzitso cha miyambo yanu? 4Pakuti °Mulungu analamulira nanena2, Lemekeza atate wako ndi3 amako; ndipo, iye wolankhulira atate wake ndi amake zoipa4, aphedwe. 5Koma inu munena, Aliyense amene adzanena kwa atate wake kapena amake, Imeneyi ndi mphatso5, chilichonse chimene [chizalandiridwa] kuchoka kwa Ine sichidzakupindulirani: 6ndipo mwanjira ina iliyonse salemekeza atate wake ndi amake; ndipo mwapeputsa lamulo la °Mulungu potsata chiphunzitso cha miyambo yanu. 7Onyenga inu! Mneneri Yesaya analosera bwino lomwe zokhudza inu, ponena6 kuti, 8Anthu awa andilemekeza ine ndi milomo yawo, koma mitima yawo ili kutali ndi Ine; 9komatu andilambira Ine kwachabe, kuphunzitsa [monga] maphunzitso a malamulo a anthu. 10Ndipo anadziitanira [Iye] khamu, nanena nawo, Imvani ndipo mumvetsetse: 11Sikuti chimene chimalowa mkwamwa mwa munthu chimamuipitsa munthuyo; koma chimene chimatuluka mkamwa mwa munthu ndi chomwe chimamuipitsa.
12Pamenepo ophunzira ake, anabwera, nanena kwa Iye, Kodi simukudziwa kuti Afarisi, pakumva mau amenewa7, akhumudwa8 nawo? 13Koma Iye poyankha anati, Mbewu iliyonse imene Atate wanga wakumwamba sanaidzale izadzulidwa. 14Alekeni choncho; iwowa ndi atsogoleri akhungu: koma ngati wakhungu atsogolera wakhungu, onsewa adzagwera m'mbuna. 15Ndipo Petro pakuyankha ananena kwa Iye, Titanthauzireni fanizo limeneli. 16Koma Iye anati, Kodi inunso muli opanda nzeru? 17Simudziwa kodi, kuti chilichonse cholowa mkamwa chimapita m'mimba, ndipo chimatayidwa kuthengo? 18Koma zinthu zonse zimene zimatuluka m'kamwa zimachokera mu mtima, ndipo zimenezi ndizo zimaipitsa munthu9. 19Pakuti mu mtima mumachokera malingaliro oipa, zakupha, zachigololo, zachiwerewere, zakuba, zochitira umboni wabodza, zamwano; 20zimenezi ndi zinthu zimene zimaipitsa munthu10.
121Ndipo Yesu, pakupita kuchokera kumeneko, anapita mkati11 mwa mbali ya ku Turo ndi Sidoni; 22ndipo taonani, mzimayi wa ku Kanani, akuchokera ku malire amenewo, anafuula [kwa iye] nanena, ndichitireni chifundo ine, Ambuye, Mwana wa Davide; mwana wanga wagwidwa koopsa ndi ziwanda. 23Komatu Iye sanamuyankhe kanthu mzimayiyu. Ndipo ophunzira ake anadza kwa [iye] namfunsa, nati, M'chotseni uyu, pakuti akulilira kumbuyo kwathu. 24Koma Iye pakuyankha anati, Inetu sindinatumidwe koma kudzapulumutsa nkhosa zosokera za m'nyumba ya Israyeli. 25Komatu iye anadza namlambira, nanena, Ambuye, ndithandizeni. 26Koma Iye poyankha anati, Sikoyenera kutenga mkate wa ana ndi kuponyera tiagalu12. 27Koma iye anati, Indetu13, Ambuye; pakuti ngakhale agalu amadya nyenyetswa zimene zikugwa kuchokera pa gome la mbuye wawo. 28Pamenepo Yesu poyankha ananena kwa iye, Mzimayi iwe, chikhulupiriro chako, [ndi] chachikulu. Zikhale momwemo kwa iwe monga ufuna. Ndipo mwana wake wa mkazi anachiritsidwa kuchokera nthawi yomweyo.
29Ndipo Yesu, pakuchoka kumeneko, anafika mbali ya kufupi ndi nyanja ya Galileya, ndipo anakwera ku phiri nakhala pansi kumeneko; 30ndipo makamu a anthu anabwera kwa Iye, ali nawo anthu olumala miyendo, osaona, osalankhula, opuwala ziwalo, ndi ena ambiri, ndipo anawaika pa mapazi ake, ndipo Iye anawachiritsa iwo: 31kotero makamu a anthu anali ozizwa poona osalankhula akulankhula, opuwala ziwalo akuchiritsidwa, olumala miyendo akuyenda, ndi osaona akuona; ndipo iwo analemekeza °Mulungu wa Israyeli. 32Koma Yesu atadziyitanira ophunzira ake kwa [Iye], anati, Ine ndili ndi chifundo ndi khamuli, chifukwa akhala ali ndi Ine kwa masiku atatu tsopano ndipo alibe chakudya chili chonse kuti adye, ndipo sindingawachotse kuno iwo asanadye kuopa kuti mwina14 angakomoke panjira. 33Ndipo ophunzira ake anati kwa Iye, Kodi tikapeza kuti mikate yochuluka muno m'chipululu imene ikhoza kukwanira khamu lalikulu lotere? 34Ndipo Yesu anati kwa iwo, Kodi muli ndi mikate ingati? Koma iwo anati, Isanu ndi iwiri, komanso nsomba zochepa. 35Ndipo Iye analamulira makamuwo kuti akhale pansi; 36ndipo atatenga mikate isanu ndi iwiri ndi nsombazo, anayamika, nainyema [iyo] ndipo anaipereka [iyo] kwa ophunzira ake, ndipo ophunzira anaipereka kwa khamulo. 37Ndipo onse anadya nakhuta; ndipo anasonkhanitsa makombo otsala ndipo anakwanira mitanga15 yodzadza isanu ndi iwiri; 38koma iwo amene anadya anali amuna zikwi zinayi, osaphatikizapo akazi ndi ana. 39 Ndipo, atawachotsa makamu aja, Iye anakwera m'ngalawa ndipo anafika ku malire a Magadani.
1 Kapena 'miyambo ya akuluakulu.'
2 Eks. 20.12.
3 Eks. 21.17.
4 Kapena 'chipongwe,' 'matemberero.'
5 chitsanzo; chopereka kwa Mulungu, onani Marko 7.11 ndi mfundo pa Mat. 27.6.
6 Yes. 29.13.
7 Kwenikweni 'awa.'
8 Monga mutu 13.57. ndiponso, paliponse pamene mau akuti 'kukhumudwa' achitika.
9 Kapena 'mwamuna.'
10 Kapena 'mwamuna.'
11 Eis. Osati kwenikweni mozungulira deralo, koma mkati mwa malowo. Mwina mwake tikhoza kutanthauzira kuti 'mkatikati mwa deralo,' kungoti ndi malo aufulu pang'ono. Mkaziyo anachokera ku dziko la Turo ndi Sidoni.
12 'Galu wamng'ono,' wocheperako kuposa 'galu' m'Chigiriki; koma mchingerezi 'tiagalu' ndi osiyaniranako. Sindinganene kuti 'galu wosayenda,' kuopa kuti akhoza kukhala mau amphamvu kwambiri, koma ndilibe chikayiko konse za kunyoza kwakukulu kumene mauwa amatanthauza; onaninso pa ndime 27.
13 Kapena mwina tikhoza kunena kuti 'Komabe' pamenepa, monga kuvomereza choonadi, koma kuchonderera; nai amangwiritsidwa ntchito kutsimikizira zimene zanenedwa, kapenanso kupempha, monga, zedi, m'Chingerezi timati, 'Inde, chitani chimenecho.' 'Komabe' zimaonetsa pena pake kufotokozera ichi momveka bwino, monga kuvomereza pa zimene Khristu analankhula kukhala umboni; 'koma' ngoperewera ngati titanena 'indetu.' 'Komabe' anagwiritsidwa choncho kupereka chivomerezo ndi pempho, ndipo limeneli likuonetsa ngati mphamvu ya nai. Onani Chiv. 22.20, 'Amen; ndidza.' Ngati tinena kuti 'Choonadi, Ambuye,' tikuyenera kuphatikizira 'komabe.' 'Choonadi, Ambuye, [komabe imvani] ngakhaledi.' Monga ku nai kukhala nalo khalidwe limeneli lochonderera, onani Filemoni 20, ndiponso likutengedwa ndi anthu ochuluka. Komabe nai akutsutsana ndi Ambuye, amene anati ouk, ndi kai gar akutsatira mwa chikhalidwe. Ndipo ndikuyembekeza amenewa kukhala lingaliro labwino. 'Inde, Ambuye, mukhoza kuchita chimenechi, ndithu.' Chotero ndaika mu lemba.
14 Onani Ndime pa, mutu 5.25; Marko 4.12.
15 Imakhala yaikulu kuposa 'malichero' pa mutu 16.9. Makamaka ndi 'lichero la nsomba.'