Mutu 1
1Petro, mtumwi wa Yesu Khristu, kwa alendo obalalika aku Ponto, Galatiya, Kapadokiya, Asiya, ndi Bituniya, 2osankhidwa molingana ndi kudziwiratu kwa Mulungu1 Atate, m’kuyeretsedwa mwa Mzimu, mukumvera ndi kuwazidwa kwa mwazi wa Yesu Khristu: Chisomo kwa inu ndi mtendere zichulukire.
3Adalitsike Mulungu2 ndi Atate wa Ambuye wathu Yesu Khristu, amene, molingana ndi chifundo chake chachikulu, anatiberekanso ku chiyembekezo cha moyo kudzera m’chiukitso cha Yesu Khristu kuchoka pakati pa akufa, 4kupita ku cholowa chosavunda, ndi chosadetsa, ndi chosaguga, chosungidwira inu m’miyamba, 5amene munasungidwa ndi mphamvu ya Mulungu3 kudzera mu chikhulupiliro pa chipulumutso chokonzeka kuvumbulutsidwa munyengo yotsiriza. 6Momwe mukondwera, kwa kanthawi kochepa panopa, ngatidi, mukhala m’chisoni ndi mayesero a mitundumitundu, 7kuti mayesedwe a chikhulupiliro chanu, ndiwo a mtengo wapatali kuposa golide amene amaonongeka, ngakhale amayesedwa ndi moto, akapezedwe woyenera kutamandika ndi ulemelero ndi ulemu m’chivumbulutso cha Yesu Khristu: 8amene, posamuona, mumkonda; pa ameneyo [ngakhale] tsopano simunamuyang’ana, koma munakhulupilira, munakondwera kwambiri ndi chimwemwe chosaneneka ndi kudzadzidwa ndi ulemelero, 9kulandira chitsiriziro cha chikhulupiliro chanu, chipulumutso cha miyoyo yanu. 10Zokhudza chipulumutso cha aneneri, amene ananenera za chisomo kwa inu, chofufuzidwa ndi chosakidwa; 11kusaka chiyani, kapena nthawi yotani, Mzimu wa Khristu umene unali mwa iwo unawalozera, kuchitira umboni asanachitike mazunzo amene anali kwa Khristu, ndi maulemelero akuchitika zitatha izi. 12Kwa iye amene zinavumbulutsidwa, osati kwa iwo okha koma kwa inu anatumikira zinthu zimenezo, zimene tsopano zalengezedwa kwa inu ndi iwo amene analalikira uthenga wabwino mwa Mzimu woyera, wotumidwa kuchoka kumwamba, umene angelo alakalaka kusuzumiramo. 13Pamenepo, podzimangira malingaliro anu, zisungeni poyembekezera ndi kukhulupirika kotheratu mu chisomo chimene chidzabweretsedwa kwa inu pa kuvumbulutsidwa kwa Yesu Khristu; 14monga ana akumvera, osafanizidwa ndi zilakolako zanu zakale m’kusadziwa kwanu; 15koma monga iye amene anakuyitanani ali woyera, inunso mukhale oyera m’makhalidwe anu onse; 16chifukwa kwalembedwa, Khalani oyera, pakuti ndine woyera. 17Ndipo mukamuyitana monga Atate iye amene, sayang’ana nkhope ya munthu, amaweruza molingana ndi ntchito ya aliyense, khalani mwa ulemu ndi kuopa m’masiku anu akukhala kwa kanthawi, 18podziwa kuti munawomboledwa, osati mwa zinthu zovunda monga siliva kapena golide, ku mayendedwe anu opanda phindu amene anaperekedwa ndi makolo anu, 19koma mwa mwazi wa mtengo wapatali, monga wa mwana wankhosa wopanda chilema ndi wopanda banga, mwazi wa Khristu, 20amene anadziwikiratu asanakhazikitsidwe maziko adziko lapansi, koma amene waonetsedwa kumapeto a nthawi chifukwa cha inu, 21amene mwa iye akhulupilira pa Mulungu4, amene anamuukitsa pakati pa akufa namupatsa iye ulemelero, kuti chikhulupiliro chanu ndi chiyembekezo chanu chikhale mwa Mulungu5. 22Mutayeretsa miyoyo yanu mwa kumvera ku choonadi ndi chikondi chosaperewera cha pa abale, kondanani mochititsa chidwi wina ndi mzake ndi mtima wangwiro; 23pobadwanso kwatsopano, osati ndi mbewu yakufa, koma yosafa, ndi mau a Mulungu6 amoyo komanso okhazikika. 24Chifukwa matupi onse ali ngati udzu, ndi ulemelero wake onse monga maluwa a udzu. Udzu wafota ndipo maluwa ake agwa; 25koma mau a Ambuye akhala kwamuyaya. Koma awa ndi mau amene m’uthenga wabwino alalikidwa kwa inu.
1Elohimu2Elohimu3Elohimu4Elohimu5Elohimu6Elohimu