Mutu-2
1Koma panali anenerinso onyenga pakati pa anthu, monga padzakhalanso aphunzitsi onyenga pakati panu, amene adzabweretsa ziphunzitso zonyenga zoononga, ndi kukana Ambuye amene anawagula iwo, kudzibweretsera okha chiwonongeko chofulumira; 2ndipo ochuluka adzatsatira makhalidwe awo oipa, momwemo njira ya choonadi idzachitidwa mwano. 3?Ndipo kudzera mu kusilira, ndi mawu okoma, iwo adzachitira malonda pa inu: amene chiweruzo chakalekale sichigona, ndipo chionongeko chawo sichiodzera. 4Pakuti ngati Mulungu1 sanalekerere angelo amene anachimwa, koma anawaponya iwo m’dzenje lakuya kwambiri ndipo anawamanga maunyolo a mdima kusungidwira chiweruzo; 5ndipo sanalekerere dziko lakale, koma anasunga Nowa, wachisanu ndi chitatu, mlaliki wa chilungamo, atabweretsa chigumula padziko lapansi kwa osapembedza; 6ndipo anawononga mizinda ya Sodomu ndi Gomola kuyisandutsa phulusa, nawadzudzula iwo ndi chigonjetso, nawakhazika chitsanzo kwa iwo amene akakhala moyo osapembedza; 7ndipo anapulumutsa Loti wolungamayo, wokhudzika ndi mayendedwe oipa a anthu opanda umulungu2, 8(pakuti munthu wolungamayo pakuona ndi kumva, anakhala pakati pawo, nazunza moyo wake wolungama tsiku ndi tsiku ndi ntchito [zawo] zosaweruzika,) 9Ambuye amadziwa m’mene angapulumutsire anthu aumulungu3 kutuluka m’mayesero, ndi kusunga osalungama ku tsiku la chiweruzo kuti akalangike; 10ndipo makamaka iwo akuyenda monga mwa thupi m’chilakolako chonyasa, ndi kunyodzetsa umbuye. Olimba mtima [ali iwo], ochita zofuna zawo; osachita mantha kulankhula mwa chipongwe za anthu olemekezeka: 11pamene angelo, amene ali akulu mu mphamvu, sawaneneza iwo, pamaso pa Ambuye, mlandu wopweteka. 12Koma awa, monga zilombo za moyo zopanda nzeru, zopangidwa kuti zigwidwe ndi kuphedwa, polankhula zinthu zopweteka zimene iwo alibe nazo chidziwitso, adzaonongekanso mu zoipa zawo, 13akulandira mphoto ya kusalungama; chifukwa chopembedzera zosangalatsa za kanthawi; mawanga ndi zilema, zolimbana m’chinyengo chawo chomwe, kudyera pamodzi ndi inu; 14kukhala nawo maso odzala ndi chigololo, ndipo osafuna kusiya tchimo, kukopa miyoyo yosakhazikika; okhala nawo mtima wadyera, ana a themberero; 15akusiya njira yawo yoongoka imene anapatukamo, natsatira m’njira ya Balamu [mwana] wa Beori, amene anakonda mphoto ya kusalungama; 16koma anadzudzulidwa mwa zoipa zake — bulu wosalankhula kulankhula mau a munthu kuletsa kupusa ka mneneri. 17Amenewa ndi akasupe opanda madzi, ndi nkhungu yokankhidwa ndi mphepo ya mkuntho, kwa iwo mdima wa ndiwe yani wasungidwira [kwamuyaya]. 18Mwa [kanthawi] alankhula kwambiri mau odzikweza achabe, iwo pokopeka ndi zilakolako za thupi, mwa chisokonezo, iwo amene angowathawa anthu oyenda m’mayendedwe oipa, 19kuwalonjeza iwo ufulu, pamene iwo eni ali akapolo a choipa; pakuti mwa iwo munthu wagonjetsedwa, mwa iye anabweretsedwanso mu ukapolo. 20Pakuti pothawa zoipa za dziko lapansi mwa chidziwitso cha Ambuye ndi Mpulumutsi Yesu Khristu, kulumikizidwanso, iwo agonjetsedwa ndi zimenezi, chitsiriziro chawo chidzakhala choipa kuposa poyamba. 21Pakuti kunali bwino kwa iwo kusadziwa njira ya chilungamo, kusiyana ndi kudziwa ndi kuchoka ku lamulo loyera loperekedwa kwa iwo. 22 Komatu mau a mwambi woona achitika kwa iwo: Galu wabwerera ku masanzi ake; komanso, Nkhumba yosambitsidwa ibwerera kukagubuduka m’matope.
1Elohimu2Elohimu3Elohimu