Mutu 1
1Paulo, mtumwi wa Yesu Khristu mwa chifuniro cha Mulungu, kwa oyera mtima ndi okhulupirika mwa Yesu Khristu amene ali ku1 Efeso2. 2Chisomo kwa inu ndi mtendere zochokera kwa Mulungu Atate wathu, ndi Ambuye Yesu Khristu.
3Odalitsika ali Mulungu ndi Atate wa Ambuye wathu Yesu Khristu, amene watidalitsa ife ndi3 mdalitso onse wa uzimu wa m’mwamba mwa Khristu; 4molingana ndi kutisankha ife lisanakhazikitsidwe dziko lapansi, kuti tikakhale oyera ndi opanda banga pamaso pake mwa chikondi; 5pamene anatikonzeratu4 kwa iye yekha kukhala ana oleledwa5 mwa Yesu Khristu kwa mwini yekha, molingana ndi chisangalatso chabwino cha chifuniro chake, 6ku chiyamiko cha ulemelero wa chisomo chake, chimene anatitenga ife mu kukonderedwa6 mwa Wokondedwayo: 7mwa iye tili nacho chiombolo m’mwazi wake, kukhululukidwa kwa zochimwa, molingana mwa kulemera kwa chisomo chake; 8chimene anatichulukitsira ife mu nzeru zonse, ndi chisamaliro 9natizindikiritsa ife chinsinsi cha chifuniro chake, molingana ndi chomukomera chimene anatsimikizira mwa iye yekha 10pakuti makonzedwe a chikwaniritso cha nthawi; kusonkhanitsa zinthu zonse mwa Khristu, zinthu zakumwamba ndi zinthu za padziko lapansi; mwa iye, 11ameneyo tapezamo cholowa, pokonzedweratu molingana ndi cholinga cha iye amene achita zonse molingana ndi uphungu wa chifuniro chake, 12kuti tikayamikitse ku ulemelero wake inu amene mwakhulupilira mwa Khristu: 13mwa ameneyonso mwakhulupilira, pakumva mau a choonadi, uthenga wabwino wa chipulumutso chanu; mwa amenenso, pakukhulupilira, mwasindikizidwa chizindikiro cha Mzimu Woyera wa lonjezano, 14amene ali chisonyezo cha cholowa chathu ku7 chiombolo chopezeka pa kumuyamika iye mu ulemelero wake.
15Umenenso ine, pakumva chikhulupiliro mwa Ambuye Yesu chimene chili mwa inu, ndi chikondi chimene muli nacho pa oyera mtima onse, 16sindileka kuyamika chifukwa cha inu, pokutchulani m’mapemphero anga, 17kuti Mulungu wa Ambuye wathu Yesu Khristu, Atate wa ulemelero, akupatseni mzimu wa nzeru ndi vumbulutso pa kumdziwa iye kwathunthu, 18powunikiridwa m’maso mwa mitima yanu, cholinga kuti mukadziwe chiyembekezo cha mayitanidwe ake, ndi kuti kulemera kwa ulemelero wa cholowa cha oyera mtima, 19ndi kupambana kwakukulu kwa mphamvu yake pa ife okhulupirika kuli kotani, molingana ndi mphamvu yake yolimba, 20imene anachititsa mwa Khristu pakumuukitsa iye pakati pa akufa, ndipo anamukhazika iye pansi8 kudzanja lake lamanja la zam’mwamba, 21pamwamba pa maukulu onse, ndi maulamuliro, ndi mphamvu, ndi ufumu, ndi dzina lililonse lotchulidwa, osati m’nyengo ino yokha, komanso imene ili mkudza; 22ndipo wakhazika zinthu zonse pansi pa mapazi9 ake, ndipo anampatsa iye kukhala mutu wa zonse mu mpingo, 23umene uli thupi lake, chidzalo cha iye amene akwanira zonse m’zonse:
1 kwenikweni “mu”, monga Mach. 13: 1; Chiv. 2: 1.
2 Ndizosangalatsa kunena kuti kudzera “ku Efeso” akupezeka pafupifupi mu makalata onse, alembi akhoza kuwasiya mauwa. Ena, popanda chifukwa chokwanira, ndalingalira izi ngati mtundu wa kalata imene imazungulira. Fanizirani Akol. 4: 16.
3 “Ndi” sakupereka mphamvu yake yeniyeni. Mau amene amalumikizitsa ena a en pamenepa akupereka china chake cha mphamvu ndi phindu limene likupezeka; akupereka mdalitso mwa chikhalidwe chake. Onani mfundo c, Mat. 3: 11.
4 Mauwa akutanthauzira “zokonzedweratu pachiyambi” akukhudza cholinga. Sindiwo “uphungu”, ngakhale kuti ndi “molingana ku ubwino wa chifuniro chake”, ndipo, mu ndime 11, “molingana ku cholinga chake”, ndi “molingana ku uphungu wa chifuniro chake chomwe”. Mau akuti horizo amatanthauza “kuyika chizindikiro”, “kudziwa”, monga ku Aroma 1: 4; pamenepa pro (anatikonzeratu) ndi zinthu zokonzedwa kale. Akutanthauza makamaka ku anthu, koma zikugwiritsidwa ntchito ku zinthu monga ku 1 Akor. 2: 7. Pamene akugwiritsidwa pa anthu, ku chimene anaikidwiratu nthawi zonse akuonjezedwa.
5 Kapena “umwana”, monga Agal. 4: 5.
6 “Kutitenga ife mu kukonderedwa kwake”, chitsanzo; “kutiika ife m’malo a chisomo ndi kukonderedwa”. Mau a Chigiriki akugwiritsidwa ntchito pamenepa ndi aku Luka 1: 28. “Anatilandira ife” ndi chiphunzitso chokhazikika pamenepa. “Kutionetsa ife chisomo kapena kukonderedwa” sakupereka mphamvu, ya pamenepo “Wokondedwayo” zingathe kutanthauza chabe chidacho. Ndi “mwa Wokondedwayo” kuti timalowa mu kukonderedwa. Kuwerenga kwina ndi, “kukonderedwa kapena kuvomerezeka mu chisomo, zimene wayikiza kwaulere mwa ife”.
7 Kapena “kwa”, eis. Amenewa akuposa mau akuti “mpaka”, chifukwa ali nacho cholowa m’maonekedwe ake. Fanizirani Agal. 3: 24. Akhoza kutanthauzidwa kuti “pa chiombolo”, kulumikizitsa ndi “kusindikizidwa”, m’malo mwa “kudzipereka”; ndiko kuti, “Mwasindikizidwa chizindikiro cha Mzimu Woyera wa lonjezano, (amene ndi kudzipereka kwa cholowa chathu,) pa”, etc.
8 “Anamukhazika iye pansi” ndi mfundo yoonjezera imene sikulumikizana mwa dongosolo la mau ndi zimene zikutitsogolera.
9 Onani Mas. 8: 6.