Mutu 12
1?Pamenepo tiyeninso ife, pokhala nawo mtambo waukulu wa mboni wotizungulira, potaya cholemetsa chilichonse, ndi tchimo limene limatikola ife mosavuta, tithamange ndi chipiliro mpikisano umene wayikidwa patsogolo pathu, 2kuyang’ana mokhazikika pa Yesu mtsogoleri ndi mkwaniritsi wa chikhulupiliro: ameneyo, chifukwa cha chimwemwe choyikidwa pamaso pake, anapilira mtanda, nanyoza manyazi, ndipo anayikidwa padzanja lamanja la mpando wachifumu wa Mulungu1. 3Pakuti talingalirani bwino iye amene anapilira kwambiri ndi ochimwa amene anatsutsana naye, kuti inu musaleme, kukomoka m’malingaliro anu. 4Inutu simunakane kufikira mwazi, polimbana nalo tchimo. 5Ndipo mwayiwala kulemekezedwa kumene kumalankhulidwa kwa inu monga ana: Mwana wanga, usanyozere kulanga kwa Ambuye, kapena kukomoka podzudzulidwa ndi iye; 6pakuti amene Ambuye amkonda amamlanga, ndi kumkwapula mwana aliyense amene iye amlandira. 7Inu mukapilira polangidwa, Mulungu2 achita pa inu monga ana ake; pakuti ndi mwana wotani amene atate wake samlanga? 8Koma ngati mukhala osalangidwa, monga ife tonse tinadutsamo, pamenepo ndinu zitsiru osati ana. 9Komanso ife tinali nawo atate a kuthupi monga wotilanga, ndipo tinapilira [m’menemo]; kodi sitingachite koposa kumvera Atate wa mizimu, ndi kukhala ndi moyo? 10Pakuti iwo anatilangadi kwa masiku ochepa, monga zinaoneka zabwino kwa iwo; koma iye anatipindulitsa, cholinga tikatenge gawo la chiyero chake. 11Koma palibe chilango pa nthawiyo chimaoneka chopereka chimwemwe, koma chisoni; koma zotsatira zake chimabereka chipatso cha mtendere wa chilungamo kwa iwo akuchilandira.
12Chifukwa chake kwezani m’mwamba manja amene akulendewera, ndi maondo olobodoka; 13ndipo ongolani njira za kumapazi kwanu, kuti chotsimphinacho chisabwezedwe; koma kuti m’malo mwake chichilitsidwe. 14Tsatirani mtendere ndi onse, ndi chiyero, kupanda kutero palibe amene adzaona Ambuye: 15poyang’anira kuti pasapezeke aliyense osoweka chisomo cha Mulungu3; kuti mwina muzu ulionse wa mkwiyo otumphuka ungakuvuteni [inu], ndipo ambiri angadetsedwe nawo; 16kuti mwina pangakhale wachigololo, kapena munthu wonyoza, monga Esau, amene chifukwa cha mtanda umodzi anagulitsa ukulu wake; 17pakuti inu mudziwanso kuti pofuna kutenga cholowa cha dalitso, anakanizidwa, (pakuti sanathe kupeza malo akulapa) ngakhale iye anafunitsitsa kutero moona mtima ndi misozi.
18Pakuti inu simunafike [ku phiri] kuti muligwire ndipo lonse linali loyaka moto, ndi kwakuda bii, ndi mdima, ndi mphepo ya mkuntho, 19ndi kulira kwa lipenga, ndi mfuu wa mau; umene iwo akumva, powiringula, adakana mau onenedwa kwa iwo osafunanso kuwamva: 20(pakuti sanakwanitse kupilira chimene chidalamulidwa: Ndipo ngati chirombo chikhudza phiri, chiponyedwe miyala; 21ndipo, anali oopsa maonekedwe, atero Mose, Ndili ndi mantha akulu ndi kunjenjemera kwakukulu;) 22koma inu simunafike ku phiri la Zioni; ndi kumzinda wa Mulungu4 wa moyo, Yerusalemu wa kumwamba; ndi angelo ochuluka, 23msonkhano wa zolengedwa zonse; ndi ku mkumano wa ana oyamba kubadwa [amene] analembedwa m’mwamba; ndi kwa Mulungu5, woweruza wa onse; ndi kwa mizimu ya anthu olungama oyesedwa angwiro; 24ndi kwa Yesu, mkhalapakati wa pangano latsopano; ndi kumwazi wowazidwawo, olankhula bwino lomwe kuposa Abele. 25Onetsetsani kuti musamkane iye amene alankhula. Pakuti ngati iwo sanathawe amene anamkana nafotokozera miyambo yadziko lapansi, koposa kotani ife amene tinachoka kwa iye [amene anachita chotero] kuchoka kumwamba: 26amene mau ake pamenepo anagwedeza dziko lapansi; koma tsopano iye analonjeza, nanena, Pakamodzi sindidzagwedeza dziko lapansi lokha, komanso kumwamba. 27Koma ichi pakamodzi, zionetsera kuchotsedwa kwa chimene chagwedezeka, monga chinapangidwa, kuti chimene sichinagwedezeke chikhalebe chilili. 28Chifukwa chake tiyeni, polandira ufumu wosagwedezeka, tikhale ndi chisomo, pa chimenechi timtumikire Mulungu6 pomvomereza ndi ulemu komanso mantha. 292 Pakutinso Mulungu7 wathu ndi moto wonyeketsa.
1Elohimu2Elohimu3Elohimu4Elohimu5Elohimu6Elohimu7Elohimu