Mutu 5

1Pakuti mkulu wansembe aliyense wotengedwa pakati pa anthu akhazikitsidwa pa anthu mu zinthu zokhuzana ndi Mulungu1, kuti akapereke mphatso ndi nsembe chifukwa cha machimo; 2akhoze kumva chifundo pa mbuli ndi agonthi, pakuti iye mwininso wavekedwa ndi machimo; 3ndipo, pachifukwa cha cholakwa chimenechi, iye akuyenera, ngakhale chifukwa cha anthu, komanso cha iye yekha, kudzipereka chifukwa cha machimo. 4Ndipo palibe azitengera ulemu yekha koma monga mwakuitanidwa ndi Mulungu2, monganso Aroni. 5Chomwecho Khristunso sanazilemekeza yekha kukhala mkulu wansembe; koma iye amene analankhula kwa iye, Ndiwe Mwana wanga, lero ndakubala iwe. 6Ngakhalenso monga pamalo pena anati, Ndiwe wansembe wamuyaya kolingana ndi dongosolo la Melikizedeki. 7Ameneyo m’masiku a thupi lake, atapereka mapemphero ndi mapembedzero kwa iye amene anali nako kuthekera kompulumutsa kuchoka ku imfa, ndi kulira kwakukulu ndi misozi; (ndipo iye anamveka chifukwa cha kulambira kwake;) 8ngakhale iye anali Mwana, anaphunzira kumvera ku zinthu zimene anamva nazo kuwawa; 9ndipo pamene anakonzeka waphumphu, anakhala kwa iwo onse akumvera iye, chiyambi cha chipulumutso chamuyaya; 10wotchedwa ndi Mulungu3 monga mkulu wansembe monga mwa dongosolo la Melikizedeke. 11Zokhudza iye amene tili nazo zonena zambiri za iye, ndipo zovuta kuzitanthauzira m’kulankhula [za izo], popeza mwakhala ogontha pakumva. 12Pakuti pamene mwa kanthawi munafuna kukhala aphunzitsi, munafunabe kuti wina akuphunzitseni kufunikira kwa chiyambi cha kuyankhula kwa Mulungu4, ndipo kwasanduka monga mkaka ufunikira, [ndipo] osati chakudya cholimba. 13Pakuti aliyense amene amamwa mkaka alibe ukadaulo m’mau a chilungamo, popeza adakali khanda; 14koma chakudya cholimba ndi cha anthu amene ali akuluakulu, amene, chifukwa cha chizolowezi, kulingalira kwao kumasiyanitsa pakati pa chabwino ndi choipa.

1Elohimu2Elohimu3Elohimu4Elohimu