Mutu 11

1Tsopano chikhulupiliro ndicho chidziwitso cha zinthu zoyembekezeredwa, chitsimikizo cha zinthu zosaonekera. 2Pakuti mu mphamvu ya ichi akulu achitiridwa umboni. 3Mwa chikhulupiliro ife tigwira kuti maiko anakonzedwa ndi Mau a Mulungu1, kotero kuti chimene chioneka chisatenge maonekedwe ake enieni kuchokera ku zinthu zoonekazo. 4Mwa chikhulupiliro Abeli anapereka kwa Mulungu2 nsembe yabwino kwambiri kuposa Kaini, mwa imeneyo iye anapezamo umboni wakukhala wolungama, Mulungu3 nachitira umboni ku mphatso zake, ndi mwa iyi, atafa, komabe iye alankhula. 5Mwa chikhulupiliro Enoki anauzidwa kuti sadzaona imfa; ndipo iye sanapezeke, chifukwa Mulungu4 anamsanduliza iye; pakuti asanasandulizidwe ali nawo umboni kuti anasangalatsa Mulungu5. 6Koma popanda chikhulupiliro nkosatheka kumsangalatsa [iye]. Pakuti iye amene asendera chifupi ndi Mulungu6 akuyenera kukhulupilira kuti iye alipo, ndipo kuti ndiye wakupereka mphoto kwa iwo amkufuna iye. 7Mwa chikhulupiliro Nowa, mwa mau anachenjeza zokhudza zinthu zosapenyeka, pokhala ndi mantha, anakonza chombo kupulumutsa nyumba yake; kumene anatsutsa nako dziko lapansi, ndipo anakhala wolowa mnyumba wa chilungamo chimene chili molingana ndi chikhulupiliro.

8Mwa chikhulupiliro Abrahamu, poyitanidwa, anamvera kupita kumalo amene adzalandira monga cholowa, ndipo anatuluka, osadziwa kumene akupita. 9Mwa chikhulupiliro iye anayenda monga mlendo m’thaka ya malonjezano monga dziko lachilendo, atakhala m’mahema ndi Isake komanso Yakobo, olowa nawo mnyumba pamodzi naye a pangano lomwelo; 10pakuti iye anadikira mzinda umene uli nawo maziko, amene Mulungu7 ndiye m’misiri wake komanso womanga wake. 11Mwa chikhulupilironso Sara mwini analandira mphamvu ya kubereka mbewu, ndi [kuti] anapyola zaka zake zoberekera; chiyambire anamuwerengera iye wokhulupirika amene analonjeza. 12Pameneponso kudachokera mwa m’modzi, ndi kuti m’modzi anafa, ngakhale monga nyenyezi za mlengalenga zili zochuluka, ndi monga mchenga osawerengeka umene uli m’mbali mwa nyanja.

13Onsewa anafa m’chikhulupiliro, asanalandire malonjezano, koma atawaona kuchokera chapatali ndi kuwavomereza [iwo], ndipo anavomereza kuti iwo ndi alendo ndi oyendayenda padziko lapansi. 14Pakuti iwo amene amalankhula zoterezi amaonetsera poyera kuti akufunitsitsa dziko lawo. 15Ndipo ngati iwo akumbukira pamene anatulukira, ali nawo mwayi kuti abwerere; 16koma tsopano akufuna malo abwino, amene ali, akumwamba; kumene Mulungu8 sachita nawo manyazi, kuti amutchule Mulungu9 wao; pakuti wawakonzera iwo mzinda.

17Mwa chikhulupiliro Abrahamu, [pamene] anayesedwa, anampereka Isake, ndipo iye amene analandira kwa iye yekha malonjezano anampereka [mwana] wake yekhayo wokondedwa, 18monga kwa iye amene kunanenedwa, Mwa Isake mbeu yako idzayitanidwa: 19kuwerengera kuti Mulungu10 anakhoza kumdzutsa [iye] ngakhale kuchokera pakati pa akufa, kumenenso iye anamlandira monga chiphiphiritso. 20Mwa chikhulupiliro Isaki anamdalitsa Yakobo ndi Esau kukhudza zinthu zimene zikubwera. 21Mwa chikhulupiliro Yakobo pamene amafa anadalitsa ana ake onse a Yosefe, ndipo analambira pamwamba pa ndodo yake. 22Mwa chikhulupiliro Yosefe pamene amafa anakumbukira za ana a Israyeli, ndipo anapereka lamulo lokhudza mafupa ake.

23Mwa chikhulupiliro Mose, atabadwa, anabisidwa kwa miyezi itatu ndi makolo ake, chifukwa anamuona mwanayo kuti anali wokongola; ndipo iwo sanaope chilamulo cha mfumu. 24Mwa chikhulupiliro Mose, pamene anakula msinkhu, anakana kutchulidwa mwana wa mwana wamkazi wa Farao; 25nasankha m’malo mwake kuzunzika pamodzi ndi anthu a Mulungu11 kusiyana ndi kukhala ndi zosangalatsa za uchimo za kanthawi; 26kulemekeza chitonzo cha Khristu chuma chachikulu kuposa chuma cha Aigupto, pakuti iye anali ndi ulemu wa malipiro. 27Mwa chikhulupiliro anachoka ku Aigupto, osaopa mkwiyo wa mfumu; pakuti anapilira, monga ngati kuona osaonekayo. 28Mwa chikhulupiliro anakondwerera pasaka ndi kuwazidwa kwa mwazi, kuti wakupha ana oyamba asawakhudze iwo.

29Mwa chikhulupiliro anaoloka nyanja Yofiira monga akuoloka pa nthaka youma; imene a Aigupto poyesera anamizidwapo.

30Mwa chikhulupiliro makoma a Yeriko anagwa, atazungulidwa masiku asanu ndi awiri. 31Mwa chikhulupiliro Rahabe huleyo sanaonongeke pamodzi ndi osakhulupilirawo, atawalandira azondi mwa mtendere.

32Ndipo ndilankhule chiyaninso? Pakuti nthawi idzandiperewera kulankhula za Gideoni, ndi Baraki, ndi Samsoni, ndi Yefita, ndi Davide ndi Samueli, ndi za aneneri: 33amene mwa chikhulupiliro anagonjetsa maufumu, anachita chilungamo, napeza malonjezano, natseka pakamwa mikango, 34kudzimitsa mphamvu ya moto, napulumuka ku lupanga lakuthwa, nakhala wamphamvu kuchoka m’chifooko, nakhala wa mphamvu mu nkhondo, napangitsa asilikali achilendo kugonja. 35Akazi analandira akufa awonso mwa chiukitso; ndipo ena anazunzidwa, osafuna kuvomereza kuomboledwa, kuti akapeze chiukitso chabwino; 36ndipo ena anadutsa anayesedwa ndi chitonzo ndi minyozo, inde, ndi kumangidwa ndi kuponyedwa mndende. 37Iwo anagendedwa miyala, kudulidwa pakati, anayesedwa, anafa imfa ya lupanga; anayenda m’zikopa za nkhosa, m’zikopa za mbuzi, osowa, osautsidwa, ochitidwa nkhaza, 38(amenewo dziko lapansi silinawayenera,) anayenda m’chipululu ndi m’mapiri, ndinso m’mapanga ndi m’mauna a dziko lapansi.

39Ndipo onsewa, atapeza umboni kudzera m’chikhulupiliro, sanalandire lonjezano, 40 Mulungu12 poona zinthu zina zabwino pa ife, kuti asakalungamitsidwe popanda ife.

1Elohimu2Elohimu3Elohimu4Elohimu5Elohimu6Elohimu7Elohimu8Elohimu9Elohimu10Elohimu11Elohimu12Elohimu